ZAULIMI APP

ZAULIMI APP

Making Agricultural Extension Services Easily Available

Docy

KALEREDWE KA ANA A MBUZI

KALEREDWE KA ANA A MBUZI

Kuti ana a mbuzi aleredwe bwino tiyenera kutsatira izi;

  1. Onetsetsani kuti kamwana kayamwa mkaka oyambirira pasanathe maola 24.
  2. Patulani make ndi kamwana pa gulu la mbuzi kwa sabata limodzi.
  3. Ipatseni madzi abwino nthawi zonse.
  4. Ngati mukuweta mbuzi za mkaka, mupatule ka mwana kuti kaziyamwa kawiri pa tsiku
  5. Kapatseni kamwana ka mbuzi zakudya za udzu pakatha masiku 21.
  6. Thenani tiana tatimuna tonse tomwe mukuona kuti simungasunge mbewu pakatha masiku 30 (mwezi umodzi).
  7. Kuyambira mwezi umodzi mpaka miyezi inayi, tiana tikhoza kumakadya kutchire pamodzi ndi mbuzi zina.
  8. Tisamale m’khola nthawi zonse kuti tiana tisadwale.
  9. Tipatseni tiana mankhwala a njoka za m’mimba tikakwana miyezi iwiri komanso zina zonse mwezi umodzi mvula isanayambe, ndi mwezi umodzi mvula ikatha.
  10. Mbuzi zonse za bere musazipatse mankhwala a njoka za m’mimba.
Share this Doc