ZAULIMI APP

ZAULIMI APP

Making Agricultural Extension Services Easily Available

Docy

MATENDA NDI TIZIROMBO TA NG'OMBE ZA MKAKA

MATENDA NDI TIZIROMBO TA NG’OMBE ZA MKAKA

MATENDA

ZIZINDIKIRO

KUPEWA NDI KUTETEZA

Kutupa kwa Mawere Kowonekeratu

(Clinical Mastitis)

  • Tizidutswa ta magazi owundana mu mkaka ochokera ku ng’ombeyo
  • Bere limatentha ndipo limatupa
  • Imatentha thupi
  • Imathamanga magazi
  • Chilakolako cha chakudya chimachepa
  • Madzi a m’thupi amachepa
  • Ng’ombe imaoneka yosachangamuka
  • Imatha kufa kumene.
  • Perekani mankhwala ku ng’ombe nthawi yoti sizikupereka mkaka komanso ku ng’ombe za matenda a mgonamgona a kutupa kwa bere
  • Tsatirani njira zaukhondo zokamira mkaka ndi ukhondo wa pamalo omwe ng’ombe zimakhala makamaka kumapeto a nyengo yomwe ng’ombe sizikupereka mkaka.

Kutupa kwa Mawere Kosaonekeratu

(Subclinical Mastitis)

  • Apa kusinthika kwa bere ndi mkaka sikumawonekeratu.
  • Ng’ombe imatulutsa mkaka wochepa
  • Mu bere mumapezeka tizirombo totchedwa bacteria ndipo asilikali a m’thupi amawonjezereka m’magazi.
  • Perekani mankhwala ku ng’ombe nthawi yoti sizikupereka mkaka komanso ku ng’ombe za matenda a mgonamgona a kutupa kwa bere
  • Tsatirani njira zaukhondo zokamira mkaka ndi ukhondo wa pamalo omwe ng’ombe zimakhala makamaka kumapeto a nyengo yomwe ng’ombe sizikupereka mkaka.

Matenda a kugwa a Ng’ombe za Mkaka

(Milk Fever)

  • Kutsalira kwa matumbo ovindikira mwana wang’ombe pobadwa.
  • Kuchepa kwa chilakolako cha chakudya
  • Ng’ombe imakhala chigonere
  • Kupinda khosi ndikuyang’ana kumbuyo
  • Ng’ombe imapanga chimbudzi cha ndowe zowuma
  • Thupi lake limazizira
  • Ng’ombe imasiya kubzukula
  • Imatha kufa ngati siyinathandizidwe mwamsanga.
  • Chepetsani mlingo wa mchere wa calcium mu zakudya kufika magalamu osaposera 100 pa n’gombe iliyonse patsiku makamaka kumapeto a nyengo yomwe ng’ombe sizikupereka mkaka.
  • Perekani chakudya chokhala ndi mchere wa magnesium kuti mlingo wa mchere wa calcium wa m’magazi ukhale oyenera.

Matenda a Kutentha Kwathupi a Gombe Laku Mmawa

(East Coast Fever)

  • Kuchepa kwa chilakolako cha chakudya
  • Imaoneka yosachangamuka ndi yodwalika
  • Kutentha kwa thupi mpaka 42oC
  • Imapuma mwa befu
  • Imatsekula m’mimba
  • Kutupa kwa anabere a m’makutu, a mkhwapa ndi mphechepeche
  • Imadwala kwa sabata imodzi ndipo imafa koma nthawi zina imachira pang’onopang’ono.
  • Ngombe zomwe ndi za chi Malawi zisambitsidwe dipi kawiri pa mwezi makamaka nyengo ya dzinja pamene kumakhala nthata zambiri. Ngati zili zachizungu zipititsidwe ku dipi sabata iliyonse
  • Ngati mlimi angakwanitse, zipatsidwe katemera wa matendawa yemwe mungampeze ku vetenale ku Lilongwe. Msinkhu wabwino kuzipatsa katemerayu ndi pomwe zinakali matole.

Matenda Odzadzitsa Madzi M’thumba la Mtima (Heartwater)

  • Chiweto chimangopezeka chitafa
  • Ziweto zotsalazo zimasiya kudya, zimatentha thupi ndiponso zimatsekula m’mimba
  • Ziweto zimawonetsa zizindikiro zokhudza ubongo monga kuzungulira, kutafuna, ukali, kugwa ndikufa
  • Ziweto zonse m’khola zimatha kufa.
  • Ng’ombe zisambitsidwe ku dipi kapena zipatsidwe katemera wa matendawa

Kutupa kwa Ndulu (Anaplasmosis)

  • Ng’ombe zazikulu zimadwalika nawo kwambiri kuposa zachichepere
  • Ng’ombe zimasiya kudya, zimatentha thupi ndipo zimatulutsa mkaka ochepa
  • Kuchepa kwa magazi ndipo thupi limaoneka la chikasu.
  • Kuwonda komanso kudzimbidwa
  • Kupuma mwa befu, kupoloza ndinso kudzandira
  • Sipakhala mkodzo wofiira
  • Chiweto chimafa pakatha sabata imodzi kapena kukhala ofooka nthawi yayitali.
  • Ng’ombe zisambitsidwe ku dipi kapena zipatsidwe katemera wa matendawa

Matenda Ofiiritsa Mkodzo Ndikuzunguza Bongo (Babesiosis)

  • Chiweto chimasiya kudya, chimatulutsa mkaka ochepa, chimatentha thupi.
  • Kuchepa kwa magazi komanso thupi limaoneka la chikasu
  • Imaonetsa zizindikiro za kusokonekera kwa ubongo
  • Kufiira kwa mkodzo
  • Kufa mwina kudwalika kwa masabata angapo.
  • Ng’ombe zisambitsidwe ku dipi kapena zipatsidwe katemera wa matendawa.

Matenda Ogonetsa (Sleeping Sickness)

  • Kutentha kwa thupi mpaka 41.5oC komwe kumakwera ndikutsika mmasiku ochepa
  • Kusakhazikika komanso chilakolako cha chakudya chimachepa
  • Kuchepa kwa magazi ndi kuwonda
  • Kutuluka anabere
  • Kupoloza.
  • Musadyetsere kumalo komwe ku mapezeka ntchentche zikuluzikulu
  • Yenderani ng’ombe zanu kuti muone ngati pali tizilomboti
  • Ngati ng’ombe imodzi olo ziwiri zadwala m’mwezi umodzi, zipatseni mankhwala zonse kupewa kuti zingadwale.
Share this Doc